Add parallel Print Page Options

Yehova Adzasamalira Yuda

10 Pemphani mvula kwa Yehova pa nthawi yamphukira;
    ndi Yehova amene amapanga mitambo ya mvula.
Iye amagwetsa mivumbi ya mvula kwa anthu,
    ndi kumeretsa mbewu za mʼmunda kwa aliyense.
Mafano amayankhula zachinyengo,
    owombeza mawula amaona masomphenya abodza;
amafotokoza maloto onama,
    amapereka chitonthozo chopandapake.
Choncho anthu amangoyendayenda ngati nkhosa zozunzika
    chifukwa chosowa mʼbusa.

“Ine ndawakwiyira kwambiri abusa,
    ndipo ndidzalanga atsogoleri;
pakuti Yehova Wamphamvuzonse adzasamalira
    nkhosa zake, nyumba ya Yuda,
    ndi kuwasandutsa ngati akavalo aulemerero ankhondo.
Mu Yuda mudzachokera mwala wapangodya,
    mudzachokera chikhomo cha tenti,
    mudzachokera uta wankhondo,
    mudzachokera mtsogoleri aliyense.
Onse pamodzi adzakhala ngati ngwazi zankhondo
    zoponda mʼmatope a mʼmisewu nthawi yankhondo.
Chifukwa Yehova adzakhala nawo,
    adzachita nkhondo ndi kugonjetsa okwera pa akavalo.

“Ndidzalimbitsa nyumba ya Yuda
    ndi kupulumutsa nyumba ya Yosefe.
Ndidzawabwezeretsa
    chifukwa ndawamvera chisoni.
Adzakhala ngati kuti
    sindinawakane,
chifukwa ndine Yehova Mulungu wawo
    ndipo ndidzawayankha.
Aefereimu adzakhala ngati ankhondo amphamvu
    adzasangalala ngati anthu amene amwa vinyo.
Ana awo adzaziona zimenezi ndipo adzasangalala;
    mʼmitima mwawo adzakondwa mwa Ambuye.
Ndidzaliza mluzu
    ndi kuwasonkhanitsa pamodzi.
Ndithu ndawawombola;
    adzachulukana ngati poyamba paja.
Ndinawamwaza pakati pa mitundu ina ya anthu,
    koma ku mayiko akutaliwo adzandikumbukira.
Iwo pamodzi ndi ana awo adzapulumuka,
    ndipo adzabwerera.
10 Ndidzawabweretsa kuchokera ku Igupto
    ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku Asiriya.
Ndidzawabwezera ku Giliyadi ndi ku Lebanoni,
    mpaka malo woti nʼkukhalamo adzatheratu.
11 Adzawoloka nyanja ya masautso;
    nyanja yokokoma idzagonja
    ndipo madzi onse a mu Nailo adzaphwa.
Kudzikuza kwa Asiriya kudzatha
    ndipo ndodo yaufumu ya Igupto idzathyoka.
12 Ndidzalimbitsa iwo mwa Yehova
    ndipo adzayenda mʼdzina lake,”
            akutero Yehova.

The Lord Will Care for Judah

10 Ask the Lord for rain in the springtime;
    it is the Lord who sends the thunderstorms.
He gives showers of rain(A) to all people,
    and plants of the field(B) to everyone.
The idols(C) speak deceitfully,
    diviners(D) see visions that lie;
they tell dreams(E) that are false,
    they give comfort in vain.(F)
Therefore the people wander like sheep
    oppressed for lack of a shepherd.(G)

“My anger burns against the shepherds,
    and I will punish the leaders;(H)
for the Lord Almighty will care
    for his flock, the people of Judah,
    and make them like a proud horse in battle.(I)
From Judah will come the cornerstone,(J)
    from him the tent peg,(K)
from him the battle bow,(L)
    from him every ruler.
Together they[a] will be like warriors in battle
    trampling their enemy into the mud of the streets.(M)
They will fight because the Lord is with them,
    and they will put the enemy horsemen to shame.(N)

“I will strengthen(O) Judah
    and save the tribes of Joseph.
I will restore them
    because I have compassion(P) on them.(Q)
They will be as though
    I had not rejected them,
for I am the Lord their God
    and I will answer(R) them.
The Ephraimites will become like warriors,
    and their hearts will be glad as with wine.(S)
Their children will see it and be joyful;
    their hearts will rejoice(T) in the Lord.
I will signal(U) for them
    and gather them in.
Surely I will redeem them;
    they will be as numerous(V) as before.
Though I scatter them among the peoples,
    yet in distant lands they will remember me.(W)
They and their children will survive,
    and they will return.
10 I will bring them back from Egypt
    and gather them from Assyria.(X)
I will bring them to Gilead(Y) and Lebanon,
    and there will not be room(Z) enough for them.
11 They will pass through the sea of trouble;
    the surging sea will be subdued
    and all the depths of the Nile will dry up.(AA)
Assyria’s pride(AB) will be brought down
    and Egypt’s scepter(AC) will pass away.(AD)
12 I will strengthen(AE) them in the Lord
    and in his name they will live securely,(AF)
declares the Lord.

Footnotes

  1. Zechariah 10:5 Or ruler, all of them together. / They