Add parallel Print Page Options

41 “Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba
    kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake,
    kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo?
    Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
Kodi idzachita nawe mgwirizano
    kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
Kodi udzasewera nayo ngati mbalame,
    kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
Kodi anthu adzayitsatsa malonda?
    Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga,
    kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo,
    ndipo iweyo sudzabwereranso.
Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza;
    kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
10 Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa.
    Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
11 Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere?
    Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.

12 “Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho,
    za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
13 Ndani angasende chikopa chake?
    Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
14 Ndani angatsekule kukamwa kwake,
    pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
15 Kumsana kwake kuli mizere ya mamba
    onga zishango zolumikizanalumikizana;
16 Mambawo ndi olukanalukana
    kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
17 Ndi olumikizanalumikizana;
    ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
18 Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali;
    maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
19 Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo
    mumathetheka mbaliwali zamoto.
20 Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi
    ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
21 Mpweya wake umayatsa makala,
    ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
22 Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake;
    aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
23 Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo
    ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
24 Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala,
    ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
25 Ngʼonayo ikangovuwuka,
    ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
26 Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu,
    ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
27 Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe
    ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
28 Muvi sungathe kuyithawitsa,
    miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
29 Zibonga zimakhala ngati ziputu;
    imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
30 Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo
    imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
31 Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali,
    imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
32 Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee,
    kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
33 Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho,
    nʼcholengedwa chopanda mantha.
34 Chimanyoza nyama zina zonse;
    icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”

41 [a]“Can you pull in Leviathan(A) with a fishhook(B)
    or tie down its tongue with a rope?
Can you put a cord through its nose(C)
    or pierce its jaw with a hook?(D)
Will it keep begging you for mercy?(E)
    Will it speak to you with gentle words?
Will it make an agreement with you
    for you to take it as your slave for life?(F)
Can you make a pet of it like a bird
    or put it on a leash for the young women in your house?
Will traders barter for it?
    Will they divide it up among the merchants?
Can you fill its hide with harpoons
    or its head with fishing spears?(G)
If you lay a hand on it,
    you will remember the struggle and never do it again!(H)
Any hope of subduing it is false;
    the mere sight of it is overpowering.(I)
10 No one is fierce enough to rouse it.(J)
    Who then is able to stand against me?(K)
11 Who has a claim against me that I must pay?(L)
    Everything under heaven belongs to me.(M)

12 “I will not fail to speak of Leviathan’s limbs,(N)
    its strength(O) and its graceful form.
13 Who can strip off its outer coat?
    Who can penetrate its double coat of armor[b]?(P)
14 Who dares open the doors of its mouth,(Q)
    ringed about with fearsome teeth?
15 Its back has[c] rows of shields
    tightly sealed together;(R)
16 each is so close to the next
    that no air can pass between.
17 They are joined fast to one another;
    they cling together and cannot be parted.
18 Its snorting throws out flashes of light;
    its eyes are like the rays of dawn.(S)
19 Flames(T) stream from its mouth;
    sparks of fire shoot out.
20 Smoke pours from its nostrils(U)
    as from a boiling pot over burning reeds.
21 Its breath(V) sets coals ablaze,
    and flames dart from its mouth.(W)
22 Strength(X) resides in its neck;
    dismay goes before it.
23 The folds of its flesh are tightly joined;
    they are firm and immovable.
24 Its chest is hard as rock,
    hard as a lower millstone.(Y)
25 When it rises up, the mighty are terrified;(Z)
    they retreat before its thrashing.(AA)
26 The sword that reaches it has no effect,
    nor does the spear or the dart or the javelin.(AB)
27 Iron it treats like straw(AC)
    and bronze like rotten wood.
28 Arrows do not make it flee;(AD)
    slingstones are like chaff to it.
29 A club seems to it but a piece of straw;(AE)
    it laughs(AF) at the rattling of the lance.
30 Its undersides are jagged potsherds,
    leaving a trail in the mud like a threshing sledge.(AG)
31 It makes the depths churn like a boiling caldron(AH)
    and stirs up the sea like a pot of ointment.(AI)
32 It leaves a glistening wake behind it;
    one would think the deep had white hair.
33 Nothing on earth is its equal(AJ)
    a creature without fear.
34 It looks down on all that are haughty;(AK)
    it is king over all that are proud.(AL)

Footnotes

  1. Job 41:1 In Hebrew texts 41:1-8 is numbered 40:25-32, and 41:9-34 is numbered 41:1-26.
  2. Job 41:13 Septuagint; Hebrew double bridle
  3. Job 41:15 Or Its pride is its