Add parallel Print Page Options

Mawu Oyamba

Mʼdziko la Uzi munali munthu wina, dzina lake Yobu. Munthu ameneyu anali wosalakwa ndi wolungama mtima, ankaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa. Anali ndi ana aamuna asanu ndi awiri ndi ana aakazi atatu, ndipo anali ndi nkhosa 7,000, ngamira 3,000, ngʼombe zantchito 1,000 ndi abulu aakazi 500, ndiponso anali ndi antchito ambiri. Iye anali munthu wotchuka kwambiri pakati pa anthu onse a mʼmayiko a kummawa.

Ana ake aamuna ankachita phwando mosinthanasinthana mʼnyumba zawo, ndipo ankayitana alongo awo atatu aja kudzadya ndi kumwa nawo. Masiku aphwandowo atatha, Yobu ankawayitana kuti adzawayeretse. Mmamawa iye ankapereka nsembe yopsereza kuperekera mwana aliyense, poganiza kuti, “Mwina ana anga achimwa ndi kutukwana Mulungu mʼmitima yawo.” Umu ndi mmene Yobu ankachitira nthawi zonse.

Yobu Ayesedwa Koyamba

Ana a Mulungu atabwera kudzadzionetsa pamaso pa Yehova, nayenso Satana anafika nawo limodzi. Yehova anati kwa Satanayo, “Kodi iwe ukuchokera kuti?”

Satana anayankha Yehova kuti, “Ndakhala ndikungoyendayenda ndi kumangozungulira mʼdzikoli.”

Pamenepo Yehova anati kwa Satana, “Kodi unalingalirapo za mtumiki wanga Yobu? Palibe wina pa dziko lapansi wofanana naye; ndi munthu wosalakwa ndi wolungama mtima, munthu amene amaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa.”

Satana anayankha kuti, “Kodi Yobu amaopa Mulungu popanda chifukwa?” 10 “Kodi Inu simumamuteteza iyeyo, nyumba yake ndi zonse zimene ali nazo? Mwadalitsa ntchito ya manja ake, kotero kuti nkhosa ndi ngʼombe zake zili ponseponse mʼdzikomo. 11 Koma tatambasulani dzanja lanu ndi kukantha zonse ali nazo ndipo iyeyo adzakutukwanani ndithu pamaso panu.”

12 Yehova anati kwa Satana, “Chabwino, tsono zonse zimene ali nazo ndaziyika mʼmanja mwako, koma iye yekhayo usamukhudze.”

Pamenepo Satana anachoka pamaso pa Yehova.

13 Tsiku lina pamene ana aamuna ndi ana aakazi a Yobu ankachita phwando ndi kumwa vinyo mʼnyumba mwa mkulu wawo, 14 wamthenga anabwera kwa Yobu ndipo anati, “Ngʼombe zanu zotipula ndipo abulu anu amadya chapafupi pomwepo, 15 tsono panabwera Aseba kudzatithira nkhondo ndi kutenga zonse. Apha antchito ndi lupanga, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”

16 Iyeyo akuyankhulabe, wamthenga wina anabwera nati, “Kunagwa mphenzi ndipo yapsereza nkhosa ndi antchito anu onse, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”

17 Iyeyo akuyankhulabe, wamthenga wina anabwera nati, “Akasidi anadzigawa mʼmagulu atatu ankhondo ndipo anafika pa ngamira zanu ndi kuzitenga. Apha antchito anu onse ndi lupanga, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”

18 Iyeyo akuyankhulabe, panafikanso wamthenga wina nati, “Ana anu aamuna ndi aakazi amachita phwando ndi kumwa vinyo mʼnyumba ya mkulu wawo, 19 mwadzidzidzi chinayamba chimphepo champhamvu chochokera ku chipululu, nʼkudzawomba nyumba mbali zonse zinayi. Nyumbayo yawagwera ndipo afa, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”

20 Atamva zimenezi, Yobu anayimirira nangʼamba mkanjo wake, ndi kumeta tsitsi lake. Kenaka anadzigwetsa pansi napembedza Mulungu, 21 nati,

“Ndinatuluka maliseche mʼmimba mwa amayi anga,
    namonso mʼmanda ndidzalowa wamaliseche.
Yehova ndiye anapereka ndipo Yehova watenga;
    litamandike dzina la Yehova.”

22 Mu zonsezi, Yobu sanachimwe kapena kunena kuti, “Mulungu walakwa.”

Prologue

In the land of Uz(A) there lived a man whose name was Job.(B) This man was blameless(C) and upright;(D) he feared God(E) and shunned evil.(F) He had seven sons(G) and three daughters,(H) and he owned seven thousand sheep, three thousand camels, five hundred yoke of oxen and five hundred donkeys,(I) and had a large number of servants.(J) He was the greatest man(K) among all the people of the East.(L)

His sons used to hold feasts(M) in their homes on their birthdays, and they would invite their three sisters to eat and drink with them. When a period of feasting had run its course, Job would make arrangements for them to be purified.(N) Early in the morning he would sacrifice a burnt offering(O) for each of them, thinking, “Perhaps my children have sinned(P) and cursed God(Q) in their hearts.” This was Job’s regular custom.

One day the angels[a](R) came to present themselves before the Lord, and Satan[b](S) also came with them.(T) The Lord said to Satan, “Where have you come from?”

Satan answered the Lord, “From roaming throughout the earth, going back and forth on it.”(U)

Then the Lord said to Satan, “Have you considered my servant Job?(V) There is no one on earth like him; he is blameless and upright, a man who fears God(W) and shuns evil.”(X)

“Does Job fear God for nothing?”(Y) Satan replied. 10 “Have you not put a hedge(Z) around him and his household and everything he has?(AA) You have blessed the work of his hands, so that his flocks and herds are spread throughout the land.(AB) 11 But now stretch out your hand and strike everything he has,(AC) and he will surely curse you to your face.”(AD)

12 The Lord said to Satan, “Very well, then, everything he has(AE) is in your power, but on the man himself do not lay a finger.”(AF)

Then Satan went out from the presence of the Lord.

13 One day when Job’s sons and daughters(AG) were feasting(AH) and drinking wine at the oldest brother’s house, 14 a messenger came to Job and said, “The oxen were plowing and the donkeys were grazing(AI) nearby, 15 and the Sabeans(AJ) attacked and made off with them. They put the servants to the sword, and I am the only one who has escaped to tell you!”

16 While he was still speaking, another messenger came and said, “The fire of God fell from the heavens(AK) and burned up the sheep and the servants,(AL) and I am the only one who has escaped to tell you!”

17 While he was still speaking, another messenger came and said, “The Chaldeans(AM) formed three raiding parties and swept down on your camels and made off with them. They put the servants to the sword, and I am the only one who has escaped to tell you!”

18 While he was still speaking, yet another messenger came and said, “Your sons and daughters(AN) were feasting(AO) and drinking wine at the oldest brother’s house, 19 when suddenly a mighty wind(AP) swept in from the desert and struck the four corners of the house. It collapsed on them and they are dead,(AQ) and I am the only one who has escaped to tell you!(AR)

20 At this, Job got up and tore his robe(AS) and shaved his head.(AT) Then he fell to the ground in worship(AU) 21 and said:

“Naked I came from my mother’s womb,
    and naked I will depart.[c](AV)
The Lord gave and the Lord has taken away;(AW)
    may the name of the Lord be praised.”(AX)

22 In all this, Job did not sin by charging God with wrongdoing.(AY)

Footnotes

  1. Job 1:6 Hebrew the sons of God
  2. Job 1:6 Hebrew satan means adversary.
  3. Job 1:21 Or will return there