Add parallel Print Page Options

Israeli ndi Nkhutukumve

48 “Mverani izi, inu nyumba ya Yakobo,
    inu amene amakutchani dzina lanu Israeli,
    ndinu a fuko la Yuda,
inu mumalumbira mʼdzina la Yehova,
    ndi kupemphera kwa Mulungu wa Israeli,
    ngakhale osati mʼchoonadi kapena mʼchilungamo.
Komabe inu mumadzitcha nzika za mzinda wopatulika
    ndipo mumadalira Mulungu wa Israeli,
    amene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse:
Zimene zinachitika poyamba ndinalosera kalekale,
    zinatuluka mʼkamwa mwanga ndipo ndinazilengeza;
    tsono mwadzidzidzi ndinachitapo kanthu ndipo zinachitikadi.
Pakuti Ine ndinadziwa kuti iwe ndiwe nkhutukumve
    wa nkhongo gwaa,
    wa mutu wowuma.
Ine ndinakuwuziratu zinthu izi kalekale lomwe;
    zisanachitike ndinazilengezeratu kwa iwe
kuti unganene kuti,
    ‘Fano langa ndilo lachita zimenezi,
    kapena kuti fano langa losema ndi kamulungu kanga kachitsulo ndiwo analamula kuti zimenezi zichitike.’
Inu munamva zinthu zimenezi.
    Kodi inu simungazivomereze?

“Kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo ndidzakuwuzani zinthu zatsopano
    zinthu zobisika zimene simunazidziwe konse.
Zinthu zimenezi zikulengedwa tsopano lino, osati kalekale;
    munali musanazimve mpaka lero lino.
Choncho inu simunganene kuti,
    ‘Zimenezi ndiye ayi, ndinazidziwa kale.’
Inu simunazimvepo kapena kuzidziwa;
    makutu anu sanali otsekuka.
Tsono Ine ndinadziwa bwino kuti ndinu anthu achiwembu ndi kuti
    chiyambire ubwana wanu munatchedwa owukira.
Ine ndikuchedwetsa mkwiyo wanga chifukwa cha dzina langa.
    Ndikukulezerani ukali wanga kuti anthu andilemekeze.
    Sindidzakuwonongani kotheratu.
10 Taonani, ndinakuyeretsani ngati siliva;
    ndinakuyesani mʼngʼanjo yamasautso.
11 Chifukwa cha ulemu wanga, chifukwa cha ulemu wanga Ine ndikuchita zimenezi.
    Ndingalole bwanji kuti ndinyozeke?
    Ulemerero wanga sindidzawupereka kwa wina.

Kumasulidwa kwa Israeli

12 “Tamvera Ine, iwe Yakobo,
    Israeli, amene ndinakuyitana:
Mulungu uja Woyamba
    ndi Wotsiriza ndine.
13 Inde dzanja langa linamanga maziko a dziko lapansi,
    dzanja langa lamanja linafunyulula mlengalenga.
Ndi mawu anga ndinalenga kumwamba
    ndi dziko lapansi.

14 “Sonkhanani pamodzi inu nonse ndipo mvetserani:
    Ndani mwa mafano anu amene analoseratu za zinthu izi?
Wokondedwa wa Yehova uja adzachita
    zomwe Iye anakonzera Babuloni;
    dzanja lake lidzalimbana ndi Kaldeya.
15 Ine, Inetu, ndayankhula;
    ndi kumuyitana
ndidzamubweretsa ndine
    ndipo adzakwaniritsa zolinga zake.

16 “Bwerani pafupi ndipo mvetserani izi:

“Kuyambira pachiyambi sindinayankhule mobisa;
    pa nthawi imene zinkachitika zimenezi Ine ndinali pomwepo.”

Ndipo tsopano Ambuye Yehova wandipatsa Mzimu wake
    ndi kundituma.

17 Yehova, Mpulumutsi wanu,
    Woyerayo wa Israeli akuti,
“Ine ndine Yehova Mulungu wanu,
    amene ndimakuphunzitsa kuti upindule,
    ndimakutsogolera pa njira yoyenera kuyitsata.
18 Ngati iwe ukanangosamalira zolamulira zanga,
    bwenzi mtendere wako ukanakhala ngati mtsinje,
    ndi chipulumutso chako ngati mafunde a pa nyanja.
19 Zidzukulu zako zikanachuluka ngati mchenga,
    ana ako akanachuluka ngati fumbi;
dzina lawo silikanachotsedwa pamaso panga
    ndipo silikanafafanizidwa konse.”

20 Tulukani mʼdziko la Babuloni!
    Thawani dziko la Kaldeya!
Lengezani zimenezi ndi mawu a chisangalalo
    ndipo muzilalikire
mpaka kumathero a dziko lapansi;
    muzinena kuti, “Yehova wawombola Yakobo mtumiki wake.”
21 Iwo sanamve ludzu pamene Yehova ankawatsogolera mʼchipululu;
    anawapatsa madzi otuluka mʼthanthwe;
anangʼamba thanthwelo ndipo
    munatuluka madzi.

22 “Palibe mtendere kwa anthu ochimwa,” akutero Yehova.

Stubborn Israel

48 “Listen to this, you descendants of Jacob,
    you who are called by the name of Israel(A)
    and come from the line of Judah,(B)
you who take oaths(C) in the name of the Lord(D)
    and invoke(E) the God of Israel—
    but not in truth(F) or righteousness—
you who call yourselves citizens of the holy city(G)
    and claim to rely(H) on the God of Israel—
    the Lord Almighty is his name:(I)
I foretold the former things(J) long ago,
    my mouth announced(K) them and I made them known;
    then suddenly(L) I acted, and they came to pass.
For I knew how stubborn(M) you were;
    your neck muscles(N) were iron,
    your forehead(O) was bronze.
Therefore I told you these things long ago;
    before they happened I announced(P) them to you
so that you could not say,
    ‘My images brought them about;(Q)
    my wooden image and metal god ordained them.’
You have heard these things; look at them all.
    Will you not admit them?

“From now on I will tell you of new things,(R)
    of hidden things unknown to you.
They are created(S) now, and not long ago;(T)
    you have not heard of them before today.
So you cannot say,
    ‘Yes, I knew(U) of them.’
You have neither heard nor understood;(V)
    from of old your ears(W) have not been open.
Well do I know how treacherous(X) you are;
    you were called a rebel(Y) from birth.
For my own name’s sake(Z) I delay my wrath;(AA)
    for the sake of my praise I hold it back from you,
    so as not to destroy you completely.(AB)
10 See, I have refined(AC) you, though not as silver;
    I have tested(AD) you in the furnace(AE) of affliction.
11 For my own sake,(AF) for my own sake, I do this.
    How can I let myself be defamed?(AG)
    I will not yield my glory to another.(AH)

Israel Freed

12 “Listen(AI) to me, Jacob,
    Israel, whom I have called:(AJ)
I am he;(AK)
    I am the first and I am the last.(AL)
13 My own hand laid the foundations of the earth,(AM)
    and my right hand spread out the heavens;(AN)
when I summon them,
    they all stand up together.(AO)

14 “Come together,(AP) all of you, and listen:
    Which of the idols has foretold(AQ) these things?
The Lord’s chosen ally(AR)
    will carry out his purpose(AS) against Babylon;(AT)
    his arm will be against the Babylonians.[a]
15 I, even I, have spoken;
    yes, I have called(AU) him.
I will bring him,
    and he will succeed(AV) in his mission.

16 “Come near(AW) me and listen(AX) to this:

“From the first announcement I have not spoken in secret;(AY)
    at the time it happens, I am there.”

And now the Sovereign Lord(AZ) has sent(BA) me,
    endowed with his Spirit.(BB)

17 This is what the Lord says—
    your Redeemer,(BC) the Holy One(BD) of Israel:
“I am the Lord your God,
    who teaches(BE) you what is best for you,
    who directs(BF) you in the way(BG) you should go.
18 If only you had paid attention(BH) to my commands,
    your peace(BI) would have been like a river,(BJ)
    your well-being(BK) like the waves of the sea.
19 Your descendants(BL) would have been like the sand,(BM)
    your children like its numberless grains;(BN)
their name would never be blotted out(BO)
    nor destroyed from before me.”

20 Leave Babylon,
    flee(BP) from the Babylonians!
Announce this with shouts of joy(BQ)
    and proclaim it.
Send it out to the ends of the earth;(BR)
    say, “The Lord has redeemed(BS) his servant Jacob.”
21 They did not thirst(BT) when he led them through the deserts;
    he made water flow(BU) for them from the rock;
he split the rock
    and water gushed out.(BV)

22 “There is no peace,”(BW) says the Lord, “for the wicked.”(BX)

Footnotes

  1. Isaiah 48:14 Or Chaldeans; also in verse 20