Add parallel Print Page Options

Yehova akuti, “ ‘Pa nthawi imeneyo, mafupa a mafumu ndi a akuluakulu a ku Yuda, mafupa a ansembe ndi a aneneri, ndiponso mafupa a anthu a ku Yerusalemu adzafukulidwa. Adzawamwaza pa nthaka kuyangʼana dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zonse zamlengalenga, zimene ankazikonda, kuzitumikira ndi kuzitsatira, kupemphako nzeru ndiponso kuzilambira. Mafupawo sadzawasonkhanitsa kapena kuwakwirira, koma adzakhala ngati ndowe pamwamba pa nthaka. Otsala onse a mtundu woyipawu adzafuna imfa kopambana moyo kulikonse kumene ndidzawapirikitsirako, akutero Yehova Wamphamvuzonse.’ ”

Tchimo ndi Chilango Chake

“Tsono awuze anthuwa, ‘Yehova akuti:

“ ‘Kodi anthu akagwa sangadzukenso?
    Munthu akasochera kodi sangathe kubwereranso?
Chifukwa chiyani nanga anthu awa akupitirirabe kuchimwa, osabwerera?
    Chifukwa chiyani Yerusalemu akubwerera mʼmbuyo?
Iwo akangamira chinyengo;
    akukana kubwerera.
Ine ndinatchera khutu kumvetsera
    koma iwo sanayankhulepo zoona.
Palibe woyipa amene analapapo zoyipa zake,
    nʼkumati, ‘Ine ndachita chiyani?’
Aliyense akutsatira njira yake
    ngati kavalo wothamangira nkhondo.
Mbalame yotchedwa kakowa ija imadziwa
    nthawi yake mlengalenga.
Koma nkhunda, namzeze ndi chingalu
    zimadziwa nthawi yonyamukira ulendo,
koma anthu anga sadziwa
    malamulo a Yehova.

“ ‘Inu mukunena bwanji kuti,
    ‘Ndife anzeru ndipo timasunga malamulo a Yehova?’
Koma ndi alembi anu
    amene akulemba zabodza.
Anthu anzeru achita manyazi;
    athedwa nzeru ndipo agwidwa.
Iwo anakana mawu a Yehova.
    Nanga tsono nzeru zawo ziwapinduliranji?
10 Nʼchifukwa chake akazi awo ndidzawapereka kwa amuna ena
    ndipo minda yawo ndidzayipereka kwa amene adzawagonjetse.
Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu,
    onse ali ndi khalidwe lofuna kupeza chuma mwakuba.
Aneneri pamodzi ndi ansembe omwe,
    onse amachita zachinyengo.
11 Iwo amapoletsa zilonda za anthu anga
    pamwamba chabe
nʼkumati, ‘Mtendere, mtendere,’
    pamene palibe mtendere.
12 Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazi?
    Ayi, alibe manyazi ndi pangʼono pomwe;
    iwo sadziwa nʼkugwetsa nkhope komwe.
Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale;
    adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalanga,
            akutero Yehova.

13 “ ‘Ndidzatenga zokolola zawo,
    Sipadzakhalanso mphesa pa mpesa
kapena nkhuyu pa mkuyu,
    ndipo masamba ake adzawuma.
Zinthu zimene ndinawapatsa
    ndidzawachotsera.’ ”

14 Koma amati, “Tikukhala pano chifukwa chiyani?
    Tiyeni tonse pamodzi
tithawire ku mizinda yotetezedwa
    ndi kukafera kumeneko.
Pakuti Yehova Mulungu wathu watsimikiza kuti tiyenera kufa.
    Watipatsa madzi aululu kuti timwe,
    chifukwa tamuchimwira.
15 Tinkayembekezera mtendere
    koma palibe chabwino chomwe chinachitika,
tinkayembekezera kuchira
    koma tinakumana ndi zoopsa zokhazokha.
16 Kulira kwa ngʼombe zazimuna za mdani
    kukumveka kuchokera ku Dani;
dziko lonse likunjenjemera
    chifukwa cha kulira kwa akavalowo.
Akubwera kudzawononga dziko
    ndi zonse zimene zili mʼmenemo.
    Adzawononga mzinda ndi onse okhalamo.”

17 Yehova akuti, “Onani, ndikukutumizirani njoka zaululu,
    mphiri zimene munthu sangathe kuzilodza,
    ndipo zidzakulumani,”

18 Ndadzazidwa ndi chisoni kwambiri,
    mtima wanga walefukiratu.
19 Imvani kulira kwa anthu anga
    kuchokera ku dziko lakutali:
akuti, “Kodi Yehova sali ku Ziyoni?
    Kodi mfumu yake sili kumeneko?”

“Chifukwa chiyani akundiputa ndi mafano awo osema,
    ndi milungu yawo yachilendo?”

20 “Nthawi yokolola yapita,
    chilimwe chapita,
    koma sitinapulumuke.”

21 Chifukwa cha mavuto a anthu anga, ine ndikumva kuwawa;
    ndikungolira ndipo mantha aakulu andigwira.
22 Kodi ku Giliyadi kulibe mankhwala ochiritsa?
    Kodi kumeneko kulibe singʼanga?
Nanga chifukwa chiyani mabala
    a anthu anga sanapole?

“‘At that time, declares the Lord, the bones of the kings and officials of Judah, the bones of the priests and prophets, and the bones(A) of the people of Jerusalem will be removed(B) from their graves. They will be exposed to the sun and the moon and all the stars of the heavens, which they have loved and served(C) and which they have followed and consulted and worshiped.(D) They will not be gathered up or buried,(E) but will be like dung lying on the ground.(F) Wherever I banish them,(G) all the survivors of this evil nation will prefer death to life,(H) declares the Lord Almighty.’

Sin and Punishment

“Say to them, ‘This is what the Lord says:

“‘When people fall down, do they not get up?(I)
    When someone turns away,(J) do they not return?
Why then have these people turned away?
    Why does Jerusalem always turn away?
They cling to deceit;(K)
    they refuse to return.(L)
I have listened(M) attentively,
    but they do not say what is right.
None of them repent(N) of their wickedness,
    saying, “What have I done?”
Each pursues their own course(O)
    like a horse charging into battle.
Even the stork in the sky
    knows her appointed seasons,
and the dove, the swift and the thrush
    observe the time of their migration.
But my people do not know(P)
    the requirements of the Lord.

“‘How can you say, “We are wise,
    for we have the law(Q) of the Lord,”
when actually the lying pen of the scribes
    has handled it falsely?
The wise(R) will be put to shame;
    they will be dismayed(S) and trapped.(T)
Since they have rejected the word(U) of the Lord,
    what kind of wisdom(V) do they have?
10 Therefore I will give their wives to other men
    and their fields to new owners.(W)
From the least to the greatest,
    all are greedy for gain;(X)
prophets(Y) and priests alike,
    all practice deceit.(Z)
11 They dress the wound of my people
    as though it were not serious.
“Peace, peace,” they say,
    when there is no peace.(AA)
12 Are they ashamed of their detestable conduct?
    No, they have no shame(AB) at all;
    they do not even know how to blush.
So they will fall among the fallen;
    they will be brought down when they are punished,(AC)
says the Lord.(AD)

13 “‘I will take away their harvest,
declares the Lord.
    There will be no grapes on the vine.(AE)
There will be no figs(AF) on the tree,
    and their leaves will wither.(AG)
What I have given them
    will be taken(AH) from them.[a]’”

14 Why are we sitting here?
    Gather together!
Let us flee to the fortified cities(AI)
    and perish there!
For the Lord our God has doomed us to perish
    and given us poisoned water(AJ) to drink,
    because we have sinned(AK) against him.
15 We hoped for peace(AL)
    but no good has come,
for a time of healing
    but there is only terror.(AM)
16 The snorting of the enemy’s horses(AN)
    is heard from Dan;(AO)
at the neighing of their stallions
    the whole land trembles.(AP)
They have come to devour(AQ)
    the land and everything in it,
    the city and all who live there.

17 “See, I will send venomous snakes(AR) among you,
    vipers that cannot be charmed,(AS)
    and they will bite you,”
declares the Lord.

18 You who are my Comforter[b] in sorrow,
    my heart is faint(AT) within me.
19 Listen to the cry of my people
    from a land far away:(AU)
“Is the Lord not in Zion?
    Is her King(AV) no longer there?”

“Why have they aroused(AW) my anger with their images,
    with their worthless(AX) foreign idols?”(AY)

20 “The harvest is past,
    the summer has ended,
    and we are not saved.”

21 Since my people are crushed,(AZ) I am crushed;
    I mourn,(BA) and horror grips me.
22 Is there no balm in Gilead?(BB)
    Is there no physician(BC) there?
Why then is there no healing(BD)
    for the wound of my people?

Footnotes

  1. Jeremiah 8:13 The meaning of the Hebrew for this sentence is uncertain.
  2. Jeremiah 8:18 The meaning of the Hebrew for this word is uncertain.