Add parallel Print Page Options

95 Bwerani, tiyeni timuyimbire Yehova mwachimwemwe,
    tiyeni tifuwule kwa Thanthwe la chipulumutso chathu
Tiyeni tibwere pamaso pake ndi chiyamiko
    ndipo mupembedzeni Iyeyo ndi zida zoyimbira ndi nyimbo.

Pakuti Yehova ndi Mulungu wamkulu,
    mfumu yayikulu pamwamba pa milungu yonse.
Mʼmanja mwake muli maziko ozama a dziko lapansi,
    ndipo msonga za mapiri ndi zake.
Nyanja ndi yake, pakuti anayilenga ndi Iye,
    ndipo manja ake anawumba mtunda wowuma.

Bwerani, tiyeni tiwerame pomulambira,
    tiyeni tigwade pamaso pa Yehova Mlengi wathu;
pakuti Iye ndiye Mulungu wathu
    ndipo ife ndife anthu a pabusa pake,
    ndi nkhosa za mʼdzanja lake.

Lero ngati inu mumva mawu ake,
    musawumitse mitima yanu monga momwe munachitira pa Meriba,
    monga munachitira tsiku lija pa Masa mʼchipululu.
Kumene makolo anu anandiyesa ndi kundiputa,
    ngakhale anaona zimene Ine ndinazichita.
10 Kwa zaka makumi anayi ndinali wokwiya ndi mʼbado umenewo;
    ndipo ndinati, “Iwo ndi anthu amene mitima yawo imasochera
    ndipo sanadziwe njira zanga.”
11 Choncho ndili chikwiyire, ndinalumbira kuti,
    “Iwowa sadzalowa ku malo anga a mpumulo.”

Psalm 95

Come,(A) let us sing for joy(B) to the Lord;
    let us shout aloud(C) to the Rock(D) of our salvation.
Let us come before him(E) with thanksgiving(F)
    and extol him with music(G) and song.

For the Lord is the great God,(H)
    the great King(I) above all gods.(J)
In his hand are the depths of the earth,(K)
    and the mountain peaks belong to him.
The sea is his, for he made it,
    and his hands formed the dry land.(L)

Come, let us bow down(M) in worship,(N)
    let us kneel(O) before the Lord our Maker;(P)
for he is our God
    and we are the people of his pasture,(Q)
    the flock under his care.

Today, if only you would hear his voice,
“Do not harden your hearts(R) as you did at Meribah,[a](S)
    as you did that day at Massah[b] in the wilderness,(T)
where your ancestors tested(U) me;
    they tried me, though they had seen what I did.
10 For forty years(V) I was angry with that generation;
    I said, ‘They are a people whose hearts go astray,(W)
    and they have not known my ways.’(X)
11 So I declared on oath(Y) in my anger,
    ‘They shall never enter my rest.’”(Z)

Footnotes

  1. Psalm 95:8 Meribah means quarreling.
  2. Psalm 95:8 Massah means testing.