Masalimo 95
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
95 Bwerani, tiyeni timuyimbire Yehova mwachimwemwe,
tiyeni tifuwule kwa Thanthwe la chipulumutso chathu
2 Tiyeni tibwere pamaso pake ndi chiyamiko
ndipo mupembedzeni Iyeyo ndi zida zoyimbira ndi nyimbo.
3 Pakuti Yehova ndi Mulungu wamkulu,
mfumu yayikulu pamwamba pa milungu yonse.
4 Mʼmanja mwake muli maziko ozama a dziko lapansi,
ndipo msonga za mapiri ndi zake.
5 Nyanja ndi yake, pakuti anayilenga ndi Iye,
ndipo manja ake anawumba mtunda wowuma.
6 Bwerani, tiyeni tiwerame pomulambira,
tiyeni tigwade pamaso pa Yehova Mlengi wathu;
7 pakuti Iye ndiye Mulungu wathu
ndipo ife ndife anthu a pabusa pake,
ndi nkhosa za mʼdzanja lake.
Lero ngati inu mumva mawu ake,
8 musawumitse mitima yanu monga momwe munachitira pa Meriba,
monga munachitira tsiku lija pa Masa mʼchipululu.
9 Kumene makolo anu anandiyesa ndi kundiputa,
ngakhale anaona zimene Ine ndinazichita.
10 Kwa zaka makumi anayi ndinali wokwiya ndi mʼbado umenewo;
ndipo ndinati, “Iwo ndi anthu amene mitima yawo imasochera
ndipo sanadziwe njira zanga.”
11 Choncho ndili chikwiyire, ndinalumbira kuti,
“Iwowa sadzalowa ku malo anga a mpumulo.”
Psalm 95
New International Version
Psalm 95
1 Come,(A) let us sing for joy(B) to the Lord;
let us shout aloud(C) to the Rock(D) of our salvation.
2 Let us come before him(E) with thanksgiving(F)
and extol him with music(G) and song.
3 For the Lord is the great God,(H)
the great King(I) above all gods.(J)
4 In his hand are the depths of the earth,(K)
and the mountain peaks belong to him.
5 The sea is his, for he made it,
and his hands formed the dry land.(L)
6 Come, let us bow down(M) in worship,(N)
let us kneel(O) before the Lord our Maker;(P)
7 for he is our God
and we are the people of his pasture,(Q)
the flock under his care.
Today, if only you would hear his voice,
8 “Do not harden your hearts(R) as you did at Meribah,[a](S)
as you did that day at Massah[b] in the wilderness,(T)
9 where your ancestors tested(U) me;
they tried me, though they had seen what I did.
10 For forty years(V) I was angry with that generation;
I said, ‘They are a people whose hearts go astray,(W)
and they have not known my ways.’(X)
11 So I declared on oath(Y) in my anger,
‘They shall never enter my rest.’”(Z)
Footnotes
- Psalm 95:8 Meribah means quarreling.
- Psalm 95:8 Massah means testing.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.