Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Asafu.

77 Ndinafuwulira Mulungu kupempha thandizo;
    ndinafuwula mokweza kwa Mulungu kuti anditcherere khutu.
Pamene ndinali pa masautso ndinafunafuna Ambuye;
    usiku ndinatambasula manja mosalekeza
    ndipo moyo wanga unakana kutonthozedwa.

Ndinakumbukira Inu Mulungu, ndipo ndinabuwula;
    ndinasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unalefuka.
            Sela
Munagwira zikope zanga kuti ndisagone
    ndipo ndinavutika kwambiri kuti ndiyankhule.
Ndinaganizira za masiku akale,
    zaka zamakedzana;
Ndinakumbukira nyimbo zanga usiku.
    Mtima wanga unasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unafunsa kuti,

“Kodi Ambuye adzatikana mpaka muyaya?
    Kodi Iwo sadzaonetsanso kukoma mtima kwawo?
Kodi Chikondi chake chosatha chija chatheratu?
    Kodi malonjezo ake alephera nthawi yonse?
Kodi Mulungu wayiwala kukhala wokoma mtima?
    Kodi mu mkwiyo wake waleka chifundo chake?”

10 Ndipo ndinaganiza, “Pa izi ine ndidzapemphanso:
    zaka za dzanja lamanja la Wammwambamwamba.
11 Ine ndidzakumbukira ntchito za Yehova;
    Ine ndidzakumbukira zodabwitsa zanu za kalekale.
12 Ndidzakumbukira ntchito zanu
    ndi kulingalira zodabwitsa zanu.”

13 Njira zanu Mulungu ndi zoyera.
    Kodi ndi mulungu uti ali wamkulu kuposa Mulungu wathu?
14 Inu ndinu Mulungu wochita zodabwitsa;
    Mumaonetsera mphamvu yanu pakati pa mitundu ya anthu.
15 Ndi dzanja lanu lamphamvu munawombola anthu anu,
    zidzukulu za Yakobo ndi Yosefe.
            Sela

16 Madzi anakuonani Mulungu,
    madzi anakuonani ndipo anachita mantha;
    nyanja yozama inakomoka.
17 Mitambo inakhuthula madzi ake pansi,
    mu mlengalenga munamveka mabingu;
    mivi yanu inawuluka uku ndi uku.
18 Bingu lanu linamveka mʼmphepo ya kamvuluvulu,
    mphenzi yanu inawalitsa dziko lonse;
    dziko lapansi linanjenjemera ndi kugwedezeka.
19 Njira yanu inadutsa pa nyanja,
    njira yanu inadutsa pa madzi amphamvu,
    ngakhale zidindo za mapazi anu sizinaoneke.

20 Inu munatsogolera anthu anu ngati gulu la nkhosa
    mwa dzanja la Mose ndi Aaroni.

Psalm 77[a]

For the director of music. For Jeduthun. Of Asaph. A psalm.

I cried out to God(A) for help;
    I cried out to God to hear me.
When I was in distress,(B) I sought the Lord;
    at night(C) I stretched out untiring hands,(D)
    and I would not be comforted.(E)

I remembered(F) you, God, and I groaned;(G)
    I meditated, and my spirit grew faint.[b](H)
You kept my eyes from closing;
    I was too troubled to speak.(I)
I thought about the former days,(J)
    the years of long ago;
I remembered my songs in the night.
    My heart meditated and my spirit asked:

“Will the Lord reject forever?(K)
    Will he never show his favor(L) again?
Has his unfailing love(M) vanished forever?
    Has his promise(N) failed for all time?
Has God forgotten to be merciful?(O)
    Has he in anger withheld his compassion?(P)

10 Then I thought, “To this I will appeal:
    the years when the Most High stretched out his right hand.(Q)
11 I will remember the deeds of the Lord;
    yes, I will remember your miracles(R) of long ago.
12 I will consider(S) all your works
    and meditate on all your mighty deeds.”(T)

13 Your ways, God, are holy.
    What god is as great as our God?(U)
14 You are the God who performs miracles;(V)
    you display your power among the peoples.
15 With your mighty arm you redeemed your people,(W)
    the descendants of Jacob and Joseph.

16 The waters(X) saw you, God,
    the waters saw you and writhed;(Y)
    the very depths were convulsed.
17 The clouds poured down water,(Z)
    the heavens resounded with thunder;(AA)
    your arrows(AB) flashed back and forth.
18 Your thunder was heard in the whirlwind,(AC)
    your lightning(AD) lit up the world;
    the earth trembled and quaked.(AE)
19 Your path(AF) led through the sea,(AG)
    your way through the mighty waters,
    though your footprints were not seen.

20 You led your people(AH) like a flock(AI)
    by the hand of Moses and Aaron.(AJ)

Footnotes

  1. Psalm 77:1 In Hebrew texts 77:1-20 is numbered 77:2-21.
  2. Psalm 77:3 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here and at the end of verses 9 and 15.