Add parallel Print Page Options

118 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino;
    pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.

Israeli anene kuti:
    “Chikondi chake ndi chosatha.”
Banja la Aaroni linene kuti,
    “Chikondi chake ndi chosatha.”
Iwo amene amaopa Yehova anene kuti:
    “Chikondi chake ndi chosatha.”

Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova,
    ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
Yehova ali nane; sindidzachita mantha.
    Munthu angandichite chiyani?
Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa.
    Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.

Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova
    kusiyana ndi kudalira munthu.
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova
    kusiyana ndi kudalira mafumu.

10 Anthu a mitundu yonse anandizinga,
    koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
11 Anandizinga mbali zonse,
    koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
12 Anandizinga ngati njuchi,
    koma anatha msanga ngati moto wapaminga;
    mʼdzina la Yehova ndinawawononga.

13 Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa,
    koma Yehova anandithandiza.
14 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga;
    Iye wakhala chipulumutso changa.

15 Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano
    ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti:
“Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
16     Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba
    Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”

17 Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo
    ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
18 Yehova wandilanga koopsa,
    koma sanandipereke ku imfa.

19 Tsekulireni zipata zachilungamo,
    kuti ndifike kudzayamika Yehova.
20 Ichi ndicho chipata cha Yehova
    chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
21 Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha;
    mwakhala chipulumutso changa.

22 Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana
    wasanduka wapangodya;
23 Yehova ndiye wachita zimenezi
    ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
24 Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga;
    tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.

25 Inu Yehova, tipulumutseni;
    Yehova, tipambanitseni.
26 Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova.
    Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
27 Yehova ndi Mulungu,
    ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife.
Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu,
    mpaka ku nyanga za guwa.

28 Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani;
    Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.

29 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino;
    pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.

Psalm 118

Give thanks to the Lord,(A) for he is good;(B)
    his love endures forever.(C)

Let Israel say:(D)
    “His love endures forever.”(E)
Let the house of Aaron say:(F)
    “His love endures forever.”
Let those who fear the Lord(G) say:
    “His love endures forever.”

When hard pressed,(H) I cried to the Lord;
    he brought me into a spacious place.(I)
The Lord is with me;(J) I will not be afraid.
    What can mere mortals do to me?(K)
The Lord is with me; he is my helper.(L)
    I look in triumph on my enemies.(M)

It is better to take refuge in the Lord(N)
    than to trust in humans.(O)
It is better to take refuge in the Lord
    than to trust in princes.(P)
10 All the nations surrounded me,
    but in the name of the Lord I cut them down.(Q)
11 They surrounded me(R) on every side,(S)
    but in the name of the Lord I cut them down.
12 They swarmed around me like bees,(T)
    but they were consumed as quickly as burning thorns;(U)
    in the name of the Lord I cut them down.(V)
13 I was pushed back and about to fall,
    but the Lord helped me.(W)
14 The Lord is my strength(X) and my defense[a];
    he has become my salvation.(Y)

15 Shouts of joy(Z) and victory
    resound in the tents of the righteous:
“The Lord’s right hand(AA) has done mighty things!(AB)
16     The Lord’s right hand is lifted high;
    the Lord’s right hand has done mighty things!”
17 I will not die(AC) but live,
    and will proclaim(AD) what the Lord has done.
18 The Lord has chastened(AE) me severely,
    but he has not given me over to death.(AF)
19 Open for me the gates(AG) of the righteous;
    I will enter(AH) and give thanks to the Lord.
20 This is the gate of the Lord(AI)
    through which the righteous may enter.(AJ)
21 I will give you thanks, for you answered me;(AK)
    you have become my salvation.(AL)

22 The stone(AM) the builders rejected
    has become the cornerstone;(AN)
23 the Lord has done this,
    and it is marvelous(AO) in our eyes.
24 The Lord has done it this very day;
    let us rejoice today and be glad.(AP)

25 Lord, save us!(AQ)
    Lord, grant us success!

26 Blessed is he who comes(AR) in the name of the Lord.
    From the house of the Lord we bless you.[b](AS)
27 The Lord is God,(AT)
    and he has made his light shine(AU) on us.
With boughs in hand,(AV) join in the festal procession
    up[c] to the horns of the altar.(AW)

28 You are my God, and I will praise you;
    you are my God,(AX) and I will exalt(AY) you.

29 Give thanks to the Lord, for he is good;
    his love endures forever.

Footnotes

  1. Psalm 118:14 Or song
  2. Psalm 118:26 The Hebrew is plural.
  3. Psalm 118:27 Or Bind the festal sacrifice with ropes / and take it