Add parallel Print Page Options

BUKU LOYAMBA

Masalimo 1–41

Wodala munthu
    amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa,
kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa,
    kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.
Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova
    ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.
Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi,
    umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake
ndipo masamba ake safota.
    Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.
Sizitero ndi anthu oyipa!
    Iwo ali ngati mungu
    umene umawuluzidwa ndi mphepo.
Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo,
    kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.

Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama,
    koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.

BOOK I

Psalms 1–41

Psalm 1

Blessed is the one(A)
    who does not walk(B) in step with the wicked(C)
or stand in the way(D) that sinners take(E)
    or sit(F) in the company of mockers,(G)
but whose delight(H) is in the law of the Lord,(I)
    and who meditates(J) on his law day and night.
That person is like a tree(K) planted by streams(L) of water,(M)
    which yields its fruit(N) in season
and whose leaf(O) does not wither—
    whatever they do prospers.(P)

Not so the wicked!
    They are like chaff(Q)
    that the wind blows away.
Therefore the wicked will not stand(R) in the judgment,(S)
    nor sinners in the assembly(T) of the righteous.

For the Lord watches over(U) the way of the righteous,
    but the way of the wicked leads to destruction.(V)