Add parallel Print Page Options

Kugonana Koletsedwa

18 Yehova anawuza Mose kuti, “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ine ndine Yehova Mulungu wanu. Musamachite zomwe amachita anthu a ku Igupto kumene munkakhala kuja, ndiponso musamachite zomwe amachita anthu a ku Kanaani kumene ndikukupititsani. Musatsatire miyambo yawo. Inu muzimvera malamulo anga ndipo muzisamalitsa kutsatira malangizo anga. Ine ndine Yehova Mulungu wanu. Choncho sungani malangizo ndi malamulo anga, popeza munthu amene amvera zimenezi adzakhala ndi moyo. Ine ndine Yehova.

“ ‘Munthu aliyense asagonane ndi wachibale wake. Ine ndine Yehova.

“ ‘Usachititse manyazi abambo ako pogonana ndi amayi ako. Iwo ndi amayi ako. Usagonane nawo.

“ ‘Usagonane ndi mkazi wa abambo ako (osakhala amayi okubala). Ukatero ukuchititsa manyazi abambo ako.

“ ‘Usagonane ndi mlongo wako, mwana wamkazi wa abambo ako, kapena mwana wamkazi wa amayi ako, kaya anabadwira mʼnyumba mwanu kapena kwina.

10 “ ‘Usagonane ndi mdzukulu wako: mwana wa mwana wako wamwamuna kapena mwana wa mwana wako wamkazi. Kutero nʼkudzichotsa ulemu.

11 “ ‘Usagonane ndi mwana wamkazi wa mkazi wa abambo ako, amene abambo akowo anabereka; popeza ameneyo ndi mlongo wako.

12 “ ‘Usagonane ndi mlongo wa abambo ako; popeza ameneyo ndi thupi limodzi ndi abambo ako.

13 “ ‘Usagonane ndi mchemwali wa amayi ako chifukwa ameneyo ndi thupi limodzi ndi amayi ako.

14 “ ‘Usachititse manyazi mchimwene wa abambo ako pogonana ndi mkazi wake popeza amenewo ndi azakhali ako.

15 “ ‘Usagonane ndi mpongozi wako popeza ameneyo ndi mkazi wa mwana wako. Choncho usamuchititse manyazi.

16 “ ‘Usagonane ndi mkazi wa mchimwene wako popeza potero ukuchititsa manyazi mʼbale wakoyo.

17 “ ‘Usagonane ndi mkazi ndiponso mwana wake wamkazi. Usagonane ndi mwana wamkazi wa mwana wake wamwamuna, kapena mwana wamkazi wa mwana wake wamkazi. Amenewo ndi thupi limodzi ndi mkaziyo. Kutero ndikuchita chinthu choyipa kwambiri.

18 “ ‘Usakwatire mchemwali wa mkazi wako ndi kumagonana naye mkazi wakoyo ali moyo ngati wopikisana naye.

19 “ ‘Usamuyandikire mkazi kuti ugonane naye pa nthawi yake yosamba.

20 “ ‘Usagonane ndi mkazi wa mnzako ndi kudziyipitsa naye.

21 “ ‘Usapereke mwana wako aliyense kuti akhale nsembe yamoto kwa Moleki ndi kuyipitsa dzina la Yehova. Ine ndine Yehova.

22 “ ‘Usagonane ndi mwamuna ngati mkazi; chimenecho ndi chinthu chonyansa.

23 “ ‘Usagonane ndi nyama ndi kudziyipitsa nayo. Mkazi asadzipereke kwa nyama kuti agonane nayo. Chimenecho ndi chisokonezo.

24 “ ‘Musadzidetse ndi zinthu zimenezi chifukwa umo ndi mmene mitundu ina imene ndikuyithamangitsa pamaso panu inadzidetsera. 25 Choncho dziko linayipa ndipo ndinalilanga chifukwa cha tchimo lake. Motero dzikolo linasanza anthu ake okhalamo. 26 Koma inu mukasunge malangizo ndi malamulo anga. Mbadwa ndiponso alendo amene akukhala pakati panu asakachite china chilichonse cha zinthu zonyansazi, 27 pakuti zinthu zonsezi ndi zomwe ankachita anthu amene ankakhala mʼdzikomo inu musanafike, ndipo dziko linayipitsidwa. 28 Koma inu musachite zimenezi kuti dziko lingakusanzeni mutaliyipitsa monga linasanzira mitundu imene imakhalamo inu musanafike.

29 “ ‘Aliyense wochita zinthu zonyansa zimenezi achotsedwe pakati pa anthu anzake. 30 Choncho mverani malangizo anga oletsa kuchita miyambo yonyansayi imene ankatsatira anthu amene analipo inu musanafike ndi kudziyipitsa nayo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’ ”

Unlawful Sexual Relations

18 The Lord said to Moses, “Speak to the Israelites and say to them: ‘I am the Lord your God.(A) You must not do as they do in Egypt, where you used to live, and you must not do as they do in the land of Canaan, where I am bringing you. Do not follow their practices.(B) You must obey my laws(C) and be careful to follow my decrees.(D) I am the Lord your God.(E) Keep my decrees and laws,(F) for the person who obeys them will live by them.(G) I am the Lord.

“‘No one is to approach any close relative to have sexual relations. I am the Lord.

“‘Do not dishonor your father(H) by having sexual relations with your mother.(I) She is your mother; do not have relations with her.

“‘Do not have sexual relations with your father’s wife;(J) that would dishonor your father.(K)

“‘Do not have sexual relations with your sister,(L) either your father’s daughter or your mother’s daughter, whether she was born in the same home or elsewhere.(M)

10 “‘Do not have sexual relations with your son’s daughter or your daughter’s daughter; that would dishonor you.

11 “‘Do not have sexual relations with the daughter of your father’s wife, born to your father; she is your sister.

12 “‘Do not have sexual relations with your father’s sister;(N) she is your father’s close relative.

13 “‘Do not have sexual relations with your mother’s sister,(O) because she is your mother’s close relative.

14 “‘Do not dishonor your father’s brother by approaching his wife to have sexual relations; she is your aunt.(P)

15 “‘Do not have sexual relations with your daughter-in-law.(Q) She is your son’s wife; do not have relations with her.(R)

16 “‘Do not have sexual relations with your brother’s wife;(S) that would dishonor your brother.

17 “‘Do not have sexual relations with both a woman and her daughter.(T) Do not have sexual relations with either her son’s daughter or her daughter’s daughter; they are her close relatives. That is wickedness.

18 “‘Do not take your wife’s sister(U) as a rival wife and have sexual relations with her while your wife is living.

19 “‘Do not approach a woman to have sexual relations during the uncleanness(V) of her monthly period.(W)

20 “‘Do not have sexual relations with your neighbor’s wife(X) and defile yourself with her.

21 “‘Do not give any of your children(Y) to be sacrificed to Molek,(Z) for you must not profane the name of your God.(AA) I am the Lord.(AB)

22 “‘Do not have sexual relations with a man as one does with a woman;(AC) that is detestable.(AD)

23 “‘Do not have sexual relations with an animal and defile yourself with it. A woman must not present herself to an animal to have sexual relations with it; that is a perversion.(AE)

24 “‘Do not defile yourselves in any of these ways, because this is how the nations that I am going to drive out before you(AF) became defiled.(AG) 25 Even the land was defiled;(AH) so I punished it for its sin,(AI) and the land vomited out its inhabitants.(AJ) 26 But you must keep my decrees and my laws.(AK) The native-born and the foreigners residing among you must not do any of these detestable things, 27 for all these things were done by the people who lived in the land before you, and the land became defiled. 28 And if you defile the land,(AL) it will vomit you out(AM) as it vomited out the nations that were before you.

29 “‘Everyone who does any of these detestable things—such persons must be cut off from their people. 30 Keep my requirements(AN) and do not follow any of the detestable customs that were practiced before you came and do not defile yourselves with them. I am the Lord your God.(AO)’”