Add parallel Print Page Options

Za Kusadya Magazi

17 Yehova anawuza Mose kuti, “Uza Aaroni ndi ana ake, pamodzi ndi Aisraeli onse kuti, ‘Chimene Yehova walamula ndi ichi: Mwisraeli aliyense amene apha ngʼombe, mwana wankhosa kapena mbuzi mu msasa kapena kunja kwa msasa, mʼmalo mobwera nayo pa khomo la tenti ya msonkhano pamaso pa Yehova ndi kuyipereka kuti ikhale nsembe ya Yehova, ameneyo wapalamula mlandu wa magazi, wakhetsa magazi ndipo ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake. Izi zili choncho kuti Aisraeli azibwera ndi nyama zawo za nsembe zimene akanaphera ku malo kwina kulikonse. Aisraeli azibwera nazo nyamazo kwa Yehova, kwa wansembe wokhala pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo aziphere pomwepo kuti zikhale nsembe za chiyanjano. Wansembe awaze magazi ake pa guwa la Yehova limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo atenthe mafuta ake kuti atulutse fungo lokomera Yehova. Motero asadzapherenso nsembe fano la mbuzi limene amachita nalo zadama. Limeneli ndi lamulo la muyaya kwa iwo ndi mibado ya mʼtsogolo.’ ”

“Uwawuze kuti, ‘Mwisraeli aliyense kapena mlendo amene amakhala pakati pawo akapereka nsembe yopsereza kapena nsembe ina iliyonse popanda kubwera nayo pa khomo la tenti ya msonkhano kudzayipereka pamaso pa Yehova, munthu ameneyo achotsedwe pakati pa anthu anzake.’ ”

10 “Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala pakati panu amene adya magazi, ndidzamufulatira ndipo ndidzamuchotsa pakati pa anthu anzake. 11 Pakuti moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi, ndipo ndawupereka kwa inu kuti muzichitira mwambo wopepesera machimo a moyo wanu pa guwa. Pajatu magazi ndiwo amachotsa machimo chifukwa moyo uli mʼmenemo. 12 Choncho ndikuwawuza Aisraeli kuti, ‘Pasapezeke aliyense wa inu wodya magazi, ngakhale mlendo wokhala pakati panu.’ ”

13 “Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala pakati panu amene amasaka ndi kupha nyama zakuthengo kapena mbalame zimene amadya, ataye magazi ake pansi ndi kuwakwirira ndi dothi, 14 chifukwa moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi ake. Nʼchifukwa chake ndinawawuza Aisraeli kuti, ‘Musamadye magazi a cholengedwa chilichonse, chifukwa moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi. Aliyense wodya magaziwo ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.

15 “ ‘Munthu aliyense, kaya ndi mbadwa kapena mlendo, amene amadya chilichonse chofa chokha, kapena chojiwa ndi zirombo, achape zovala zake ndi kusamba, komabe adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Kenaka adzakhala woyeretsedwa. 16 Koma ngati sachapa zovala zake ndi kusamba, adzasenzabe machimo ake.’ ”

Eating Blood Forbidden

17 The Lord said to Moses, “Speak to Aaron and his sons(A) and to all the Israelites and say to them: ‘This is what the Lord has commanded: Any Israelite who sacrifices an ox,[a] a lamb(B) or a goat(C) in the camp or outside of it instead of bringing it to the entrance to the tent of meeting(D) to present it as an offering to the Lord in front of the tabernacle of the Lord(E)—that person shall be considered guilty of bloodshed; they have shed blood and must be cut off from their people.(F) This is so the Israelites will bring to the Lord the sacrifices they are now making in the open fields. They must bring them to the priest, that is, to the Lord, at the entrance to the tent of meeting and sacrifice them as fellowship offerings.(G) The priest is to splash the blood against the altar(H) of the Lord(I) at the entrance to the tent of meeting and burn the fat as an aroma pleasing to the Lord.(J) They must no longer offer any of their sacrifices to the goat idols[b](K) to whom they prostitute themselves.(L) This is to be a lasting ordinance(M) for them and for the generations to come.’(N)

“Say to them: ‘Any Israelite or any foreigner residing among them who offers a burnt offering or sacrifice and does not bring it to the entrance to the tent(O) of meeting(P) to sacrifice it to the Lord(Q) must be cut off from the people of Israel.

10 “‘I will set my face against any Israelite or any foreigner residing among them who eats blood,(R) and I will cut them off from the people. 11 For the life of a creature is in the blood,(S) and I have given it to you to make atonement for yourselves on the altar; it is the blood that makes atonement for one’s life.[c](T) 12 Therefore I say to the Israelites, “None of you may eat blood, nor may any foreigner residing among you eat blood.”

13 “‘Any Israelite or any foreigner residing among you who hunts any animal or bird that may be eaten must drain out the blood and cover it with earth,(U) 14 because the life of every creature is its blood. That is why I have said to the Israelites, “You must not eat the blood of any creature, because the life of every creature is its blood; anyone who eats it must be cut off.”(V)

15 “‘Anyone, whether native-born or foreigner, who eats anything(W) found dead or torn by wild animals(X) must wash their clothes and bathe with water,(Y) and they will be ceremonially unclean till evening;(Z) then they will be clean. 16 But if they do not wash their clothes and bathe themselves, they will be held responsible.(AA)’”

Footnotes

  1. Leviticus 17:3 The Hebrew word can refer to either male or female.
  2. Leviticus 17:7 Or the demons
  3. Leviticus 17:11 Or atonement by the life in the blood