Add parallel Print Page Options

Uthenga umene mneneri Habakuku analandira mʼmasomphenya.

Dandawulo la Habakuku

Kodi inu Yehova, ndidzakhala ndikukupemphani thandizo kwa nthawi yayitali motani,
    koma wosayankha?
Kapena kufuwulira kwa inu kuti, “Chiwawa kuno!”
    koma wosatipulumutsa?
Chifukwa chiyani mukundionetsa zinthu zoyipa?
    Chifukwa chiyani mukundionetsa mavutowa?
Ndikuona chiwonongeko ndi chiwawa;
    pali ndewu ndi kukangana kwambiri.
Kotero malamulo anu atha mphamvu,
    ndipo chilungamo sichikugwira ntchito.
Anthu oyipa aposa olungama,
    kotero apotoza chilungamo.

Yankho la Yehova

“Yangʼanani pakati pa mitundu ya anthu, ndipo penyetsetsani,
    ndipo muthedwe nazo nzeru.
Pakuti ndidzachitadi zinthu pa nthawi yanu
    zimene inu simudzazikhulupirira,
    ngakhale wina atakufotokozerani.
Pakuti taonani, Ine ndikuwutsa Ababuloni,
    anthu ankhanza ndiponso amphamvu,
amene amapita pa dziko lonse lapansi
    kukalanda malo amene si awo.
Iwowa ndi anthu ochititsa mantha, ndipo ndi owopsa;
    amadzipangira okha malamulo
    ndi kudzipezera okha ulemu.
Akavalo awo ndi aliwiro kwambiri kupambana akambuku
    ndi owopsa kupambana mimbulu yolusa nthawi ya madzulo.
Okwerapo awo akuthamanga molunjika;
    a pa akavalo awo ndi ochokera kutali,
akuwuluka ngati chiwombankhanga chofuna kugwira nyama;
    onse akubwera atakonzekera zachiwawa.
Gulu la ankhondo likubwera ngati mphepo ya mʼchipululu
    ndi kugwira akapolo ochuluka ngati mchenga.
10 Akunyoza mafumu
    ndiponso kuchitira chipongwe olamulira.
Akupeputsa mizinda yonse yotetezedwa;
    akumanga mitumbira ndi kulanda mizindayo.
11 Kenaka amasesa mofulumira ngati mphepo nʼkumangopitirirabe,
    anthu ochimwa, amene mphamvu zawo ndiye mulungu wawo.”

Dandawulo Lachiwiri la Habakuku

12 Inu Yehova, kodi sindinu wachikhalire?
    Mulungu wanga, Woyera wanga, ife sitidzafa.
Inu Yehova, munawasankha anthuwo kuti abweretse chiweruzo;
    Inu Thanthwe, munawayika iwowo kuti atilange.
13 Maso anu ndi oyera kwambiri safuna kuona choyipa;
    Inu simulekerera cholakwa.
Chifukwa chiyani nanga mukulekerera anthu ochita zachinyengowa?
    Chifukwa chiyani muli chete pamene anthu oyipa
    akuwononga anthu olungama kupambana iwowo?
14 Mwasandutsa anthu kukhala ngati nsomba zamʼnyanja,
    ngati zolengedwa zamʼnyanja zimene zilibe wolamulira.
15 Mdani wawo woyipa amakoka anthu onse ndi mbedza,
    amawakola mu ukonde wake,
amawasonkhanitsa mu khoka lake;
    kotero iyeyo amakondwa ndi kusangalala.
16 Choncho iye amaperekera nsembe ukonde wake
    ndiponso kufukizira lubani khoka lake,
popeza ukonde wakewo ndiye umamubweretsera moyo wapamwamba
    ndipo amadya chakudya chabwino kwambiri.
17 Kodi iye azipitirabe kugwiritsa ntchito makoka akewo,
    kuwononga mitundu ya anthu mopanda chifundo?

The prophecy(A) that Habakkuk the prophet received.

Habakkuk’s Complaint

How long,(B) Lord, must I call for help,
    but you do not listen?(C)
Or cry out to you, “Violence!”
    but you do not save?(D)
Why do you make me look at injustice?
    Why do you tolerate(E) wrongdoing?(F)
Destruction and violence(G) are before me;
    there is strife,(H) and conflict abounds.
Therefore the law(I) is paralyzed,
    and justice never prevails.
The wicked hem in the righteous,
    so that justice(J) is perverted.(K)

The Lord’s Answer

“Look at the nations and watch—
    and be utterly amazed.(L)
For I am going to do something in your days
    that you would not believe,
    even if you were told.(M)
I am raising up the Babylonians,[a](N)
    that ruthless and impetuous people,
who sweep across the whole earth(O)
    to seize dwellings not their own.(P)
They are a feared and dreaded people;(Q)
    they are a law to themselves
    and promote their own honor.
Their horses are swifter(R) than leopards,
    fiercer than wolves(S) at dusk.
Their cavalry gallops headlong;
    their horsemen come from afar.
They fly like an eagle swooping to devour;
    they all come intent on violence.
Their hordes[b] advance like a desert wind
    and gather prisoners(T) like sand.
10 They mock kings
    and scoff at rulers.(U)
They laugh at all fortified cities;
    by building earthen ramps(V) they capture them.
11 Then they sweep past like the wind(W) and go on—
    guilty people, whose own strength is their god.”(X)

Habakkuk’s Second Complaint

12 Lord, are you not from everlasting?(Y)
    My God, my Holy One,(Z) you[c] will never die.(AA)
You, Lord, have appointed(AB) them to execute judgment;
    you, my Rock,(AC) have ordained them to punish.
13 Your eyes are too pure(AD) to look on evil;
    you cannot tolerate wrongdoing.(AE)
Why then do you tolerate(AF) the treacherous?(AG)
    Why are you silent while the wicked
    swallow up those more righteous than themselves?(AH)
14 You have made people like the fish in the sea,
    like the sea creatures that have no ruler.
15 The wicked(AI) foe pulls all of them up with hooks,(AJ)
    he catches them in his net,(AK)
he gathers them up in his dragnet;
    and so he rejoices and is glad.
16 Therefore he sacrifices to his net
    and burns incense(AL) to his dragnet,
for by his net he lives in luxury
    and enjoys the choicest food.
17 Is he to keep on emptying his net,
    destroying nations without mercy?(AM)

Footnotes

  1. Habakkuk 1:6 Or Chaldeans
  2. Habakkuk 1:9 The meaning of the Hebrew for this word is uncertain.
  3. Habakkuk 1:12 An ancient Hebrew scribal tradition; Masoretic Text we