Add parallel Print Page Options

Kuyitanidwa kwa Ezekieli

Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, imirira kuti ndiyankhule nawe.” Pamene ankayankhula nane, Mzimu wa Mulungu unalowa mwa ine ndipo unandiyimiritsa, ndipo ndinamva Iye akundiyankhula.

Iye anati, “Iwe mwana wa munthu, Ine ndikukutuma kwa Aisraeli, mtundu wa anthu owukira umene wandiwukira Ine; Iwo ndi makolo awo akhala akundiwukira Ine mpaka lero lino. Ndikukutuma kwa anthu okanika ndiponso nkhutukumve. Ndikukutuma kuti akawawuze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena. Kaya akamva kaya sakamvera, pakuti iwo ndi anthu opanduka, komabe adzadziwa kuti mneneri ali pakati pawo. Tsono iwe mwana wa munthu, usachite nawo mantha kapena kuopa zimene azikanena. Usachite mantha, ngakhale minga ndi mkandankhuku zikuzinge ndipo ukukhala pakati pa zinkhanira. Usachite mantha ndi zimene akunena kapena kuopsedwa ndi nkhope zawo, popeza anthuwa ndi awupandu. Ukawawuze ndithu mawu anga, kaya akamva kaya sakamva. Paja anthuwa ndi awupandu. Koma iwe mwana wa munthu, mvetsera zimene ndikukuwuza. Usakhale wowukira ngati iwowo. Tsono yasama pakamwa pako kuti udye chimene ndikukupatsa.”

Nditayangʼana ndinangoona dzanja litaloza ine, litagwira mpukutu wolembedwa. 10 Anawufunyulura pamaso panga. Mpukutu wonse unali wolembedwa kuseri nʼkuseri. Ndipo mawu amene analembedwa mʼmenemo anali a madandawulo, maliro ndi matemberero.

Ezekiel’s Call to Be a Prophet

He said to me, “Son of man,[a](A) stand(B) up on your feet and I will speak to you.(C) As he spoke, the Spirit came into me and raised me(D) to my feet, and I heard him speaking to me.

He said: “Son of man, I am sending you to the Israelites, to a rebellious nation that has rebelled against me; they and their ancestors have been in revolt against me to this very day.(E) The people to whom I am sending you are obstinate and stubborn.(F) Say to them, ‘This is what the Sovereign Lord says.’(G) And whether they listen or fail to listen(H)—for they are a rebellious people(I)—they will know that a prophet has been among them.(J) And you, son of man, do not be afraid(K) of them or their words. Do not be afraid, though briers and thorns(L) are all around you and you live among scorpions. Do not be afraid of what they say or be terrified by them, though they are a rebellious people.(M) You must speak(N) my words to them, whether they listen or fail to listen, for they are rebellious.(O) But you, son of man, listen to what I say to you. Do not rebel(P) like that rebellious people;(Q) open your mouth and eat(R) what I give you.”

Then I looked, and I saw a hand(S) stretched out to me. In it was a scroll,(T) 10 which he unrolled before me. On both sides of it were written words of lament and mourning and woe.(U)

Footnotes

  1. Ezekiel 2:1 The Hebrew phrase ben adam means human being. The phrase son of man is retained as a form of address here and throughout Ezekiel because of its possible association with “Son of Man” in the New Testament.