Add parallel Print Page Options

Zoletsedwa pa Maliro

14 Inu ndinu ana a Yehova Mulungu wanu. Osamadzichekacheka kapena kudzimeta pamphumi chifukwa cha abale anu amene amwalira, pakuti ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Pakati pa anthu onse pa dziko lonse lapansi, Yehova wasankha inu kuti chikhale chuma chake chamtengo wapatali.

Musamadye chinthu chilichonse chonyansa. Nyama zomwe mukhoza kudya ndi izi: ngʼombe, nkhosa, mbuzi, mbawala, gwape, mphoyo, mphalapala, ngoma, nyumbu ndi mbalale. Nyama iliyonse imene ili ndi chipondero chogawikana pakati ndi yobzikula mukhoza kudya. Komabe pakati pa nyama zimene zimabzikula kapena zogawikana zipondero, zimene simukuyenera kudya ndi ngamira, kalulu ndi mbira. Zimenezi ngakhale zimabzikula, zipondero zake sizogawikana, choncho ndi zodetsedwa, musadye. Nkhumba simabzikula ndi yodetsedwanso ngakhale ili ndi zipondero zogawikana. Musamadye nyama yake kapena kukhudza imene yafa.

Mwa zamoyo zonse zimene zimakhala mʼmadzi, mukhoza kudya chilichonse chimene chili ndi minga ya pa msana ndi mamba. 10 Koma chilichonse chimene chilibe minga ya pa msana ndi mamba musadye pakuti nʼchodetsedwa.

11 Mukhoza kudya mbalame iliyonse yoyenera kudya. 12 Koma simukuyenera kudya izi: mphungu, nkhwazi, mwimba, 13 nankapakapa, akamtema, akhungubwi a mitundu yonse, ndi mtundu uliwonse wa miphamba, 14 mtundu uliwonse wa khwangwala, 15 kadzidzi wamphondo, kadzidzi wodzuma, chipudo, mtundu uliwonse wa akabawi, 16 kadzidzi wamngʼono, chiswankhono ndi mantchichi, 17 tsekwe, vuwo, dembo, 18 indwa, zimeza za mitundu yonse, nsadzu ndi mleme.

19 Zowuluka zonse za miyendo inayi ndi zodetsedwa. Musamadye zimenezi. 20 Koma chowuluka chilichonse choyenera kudya mukhoza kudya.

21 Musamadye chilichonse chimene mwachipeza chofaifa. Mukhoza kupatsa mlendo amene akukhala mu mzinda wina uliwonse wa mizinda yanu. Iyeyo akhoza kudya kapena mukhoza kugulitsa kwa wina aliyense amene sali wa mtundu wanu. Koma inu ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu.

Musamaphike mwana wambuzi mu mkaka wa mayi wake.

Za Chakhumi

22 Muzionetsetsa kuti mukupatula chakhumi pa zokolola zanu chaka chilichonse. 23 Muzidyera chakhumi cha tirigu wanu, vinyo wanu watsopano ndi mafuta, ndi ana oyamba kubadwa a ngʼombe zanu pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene adzasankhe ngati kokhalako dzina lake, kuti muphunzire kuopa Yehova Mulungu wanu. 24 Koma ngati malo amenewa ali kutali kwambiri ndipo kuti inu mwadalitsidwa ndi Yehova Mulungu wanu, ndipo simungathe kunyamula chakhumi chanu (chifukwa chakuti malo amene Yehova adzasankha kukayikako dzina lake ali kutali kwambiri), 25 ndiye musinthitse chakhumi chanucho ndi siliva, ndipo mutenge silivayo ndi kupita naye kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe. 26 Gwiritsani ntchito silivayo kugula chilichonse chimene muchifuna monga ngʼombe, nkhosa, vinyo kapena zakumwa zina zosasitsa, kapena china chilichonse chimene muchifuna. Ndipo inu ndi anthu a pa banja panu mudzazidyera komweko pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kukondwera. 27 Alevi okhala mʼmizinda yanu musaleke kuwathandiza popeza alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo.

28 Kumapeto kwa zaka zitatu zilizonse muzibweretsa zakhumi zonse pa zokolola za chaka chimenecho ndi kuzisunga mʼmidzi yanu, 29 kuti Alevi (amene alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo), alendo, ana ndi akazi amasiye, amene akukhala mʼmizinda yanu akhoza kubwera kudzadya ndi kukhuta. Ndipo kuti akutero Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa ntchito zanu zonse.

Clean and Unclean Food(A)

14 You are the children(B) of the Lord your God. Do not cut yourselves or shave the front of your heads for the dead, for you are a people holy(C) to the Lord your God.(D) Out of all the peoples on the face of the earth, the Lord has chosen you to be his treasured possession.(E)

Do not eat any detestable thing.(F) These are the animals you may eat:(G) the ox, the sheep, the goat,(H) the deer,(I) the gazelle, the roe deer, the wild goat,(J) the ibex, the antelope and the mountain sheep.[a] You may eat any animal that has a divided hoof and that chews the cud. However, of those that chew the cud or that have a divided hoof you may not eat the camel, the rabbit or the hyrax. Although they chew the cud, they do not have a divided hoof; they are ceremonially unclean for you. The pig is also unclean; although it has a divided hoof, it does not chew the cud. You are not to eat their meat or touch their carcasses.(K)

Of all the creatures living in the water, you may eat any that has fins and scales. 10 But anything that does not have fins and scales you may not eat; for you it is unclean.

11 You may eat any clean bird. 12 But these you may not eat: the eagle, the vulture, the black vulture, 13 the red kite, the black kite, any kind(L) of falcon,(M) 14 any kind of raven,(N) 15 the horned owl, the screech owl, the gull, any kind of hawk, 16 the little owl, the great owl, the white owl, 17 the desert owl,(O) the osprey, the cormorant, 18 the stork, any kind of heron, the hoopoe and the bat.

19 All flying insects are unclean to you; do not eat them. 20 But any winged creature that is clean you may eat.(P)

21 Do not eat anything you find already dead.(Q) You may give it to the foreigner residing in any of your towns, and they may eat it, or you may sell it to any other foreigner. But you are a people holy to the Lord your God.(R)

Do not cook a young goat in its mother’s milk.(S)

Tithes

22 Be sure to set aside a tenth(T) of all that your fields produce each year. 23 Eat(U) the tithe of your grain, new wine(V) and olive oil, and the firstborn of your herds and flocks in the presence of the Lord your God at the place he will choose as a dwelling for his Name,(W) so that you may learn(X) to revere(Y) the Lord your God always. 24 But if that place is too distant and you have been blessed by the Lord your God and cannot carry your tithe (because the place where the Lord will choose to put his Name is so far away), 25 then exchange(Z) your tithe for silver, and take the silver with you and go to the place the Lord your God will choose. 26 Use the silver to buy whatever you like: cattle, sheep, wine or other fermented drink,(AA) or anything you wish. Then you and your household shall eat there in the presence of the Lord your God and rejoice.(AB) 27 And do not neglect the Levites(AC) living in your towns, for they have no allotment or inheritance of their own.(AD)

28 At the end of every three years, bring all the tithes(AE) of that year’s produce and store it in your towns,(AF) 29 so that the Levites (who have no allotment(AG) or inheritance(AH) of their own) and the foreigners,(AI) the fatherless and the widows who live in your towns may come and eat and be satisfied,(AJ) and so that the Lord your God may bless(AK) you in all the work of your hands.

Footnotes

  1. Deuteronomy 14:5 The precise identification of some of the birds and animals in this chapter is uncertain.