Add parallel Print Page Options

Kumvera Aulamuliro

13 Aliyense ayenera kumvera akulu olamulira, chifukwa palibe ulamuliro umene sunachokere kwa Mulungu. Olamulira amene alipo anayikidwa ndi Mulungu. Kotero kuti, iwo amene awukira ulamuliro atsutsana ndi chimene Mulungu anakhazikitsa. Ndipo amene atero adzibweretsera okha chilango. Pakuti olamulira saopseza amene amachita zabwino koma amene amachita zoyipa. Kodi mukufuna kukhala osaopa olamulira? Tsono chitani zoyenera ndipo adzakuyamikirani. Pakuti iyeyo ndi mtumiki wa Mulungu wokuchitirani zabwino. Koma ngati muchita zoyipa muchite mantha, pakuti iye ali ndi mphamvu zolangira. Iye ndi mtumiki wa Mulungu wobweretsa mkwiyo ndi kulanga onse ochita zoyipa. Nʼchifukwa chake ndi koyenera kugonjera olamulira, osati chifukwa choopa kulangidwa kokha komanso chifukwa cha chikumbumtima. Ichi nʼchifukwa chakenso inu mumapereka msonkho. Pakuti olamulira ndi atumiki a Mulungu amene amapereka nthawi yawo yonse kulamulira. Mubwezereni aliyense amene munamukongola. Ngati inu muli ndi ngongole yamsonkho, perekani msonkho kwa oyenera kuwalipira. Ngati ndi kuopa perekeni kwa oyenera kuwaopa ndipo ngati ndi ulemu kwa oyenera ulemu.

Chikondi Chimakwaniritsa Malamulo

Musakhale ndi ngongole ndi wina aliyense kupatula ngongole ya kukondana wina ndi mnzake. Pakuti amene amakonda munthu mnzake wakwaniritsa lamulo. Malamulo awa: “Usachite chigololo,” “Usaphe,” “Usabe,” “Usasirire,” ndi malamulo ena onse amene alipo, akhazikika pa lamulo limodzi ili, “Konda mnansi wako monga iwe mwini.” 10 Chikondi sichichitira mnzake zoyipa. Chifukwa chake chikondi ndicho chokwaniritsa lamulo.

11 Ndipo chitani ichi pozindikira nthawi ino. Nthawi yafika yoti inu mudzuke kutulo, chifukwa chipulumutso chathu chili pafupi tsopano kuposa pamene tinayamba kukhulupirira. 12 Usiku watsala pafupifupi kutha. Kwatsala pangʼono kucha. Tiyeni tsono tichotse ntchito zamdima ndipo tivale chovala chakuwunika. 13 Tiyeni tikhale moyenera monga nthawi ya masana, osati mʼmagulu amadyerero, achiwerewere ndi kuledzera, mʼmadama ndi zonyansa komanso osati mʼmagawano ndi nsanje. 14 Koma valani Ambuye Yesu Khristu ndipo musaganizire za momwe mungakwaniritsire zokhumba zachikhalidwe cha uchimo.

Submission to Governing Authorities

13 Let everyone be subject to the governing authorities,(A) for there is no authority except that which God has established.(B) The authorities that exist have been established by God. Consequently, whoever rebels against the authority is rebelling against what God has instituted,(C) and those who do so will bring judgment on themselves. For rulers hold no terror for those who do right, but for those who do wrong. Do you want to be free from fear of the one in authority? Then do what is right and you will be commended.(D) For the one in authority is God’s servant for your good. But if you do wrong, be afraid, for rulers do not bear the sword for no reason. They are God’s servants, agents of wrath to bring punishment on the wrongdoer.(E) Therefore, it is necessary to submit to the authorities, not only because of possible punishment but also as a matter of conscience.(F)

This is also why you pay taxes,(G) for the authorities are God’s servants, who give their full time to governing. Give to everyone what you owe them: If you owe taxes, pay taxes;(H) if revenue, then revenue; if respect, then respect; if honor, then honor.

Love Fulfills the Law

Let no debt remain outstanding, except the continuing debt to love one another, for whoever loves others has fulfilled the law.(I) The commandments, “You shall not commit adultery,” “You shall not murder,” “You shall not steal,” “You shall not covet,”[a](J) and whatever other command there may be, are summed up(K) in this one command: “Love your neighbor as yourself.”[b](L) 10 Love does no harm to a neighbor. Therefore love is the fulfillment of the law.(M)

The Day Is Near

11 And do this, understanding the present time: The hour has already come(N) for you to wake up from your slumber,(O) because our salvation is nearer now than when we first believed. 12 The night is nearly over; the day is almost here.(P) So let us put aside the deeds of darkness(Q) and put on the armor(R) of light. 13 Let us behave decently, as in the daytime, not in carousing and drunkenness,(S) not in sexual immorality and debauchery, not in dissension and jealousy.(T) 14 Rather, clothe yourselves with the Lord Jesus Christ,(U) and do not think about how to gratify the desires of the flesh.[c](V)

Footnotes

  1. Romans 13:9 Exodus 20:13-15,17; Deut. 5:17-19,21
  2. Romans 13:9 Lev. 19:18
  3. Romans 13:14 In contexts like this, the Greek word for flesh (sarx) refers to the sinful state of human beings, often presented as a power in opposition to the Spirit.