Add parallel Print Page Options

Solomoni Amanga Nyumba ya Mulungu

Patapita zaka 480 Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto, chaka chachinayi cha ulamuliro wa Solomoni mu Israeli, mwezi wa Zivi, umene ndi mwezi wachiwiri, Solomoni anayamba kumanga Nyumba ya Yehova.

Nyumba imene Solomoni anamangira Yehova mulitali mwake inali mamita 27, mulifupi mwake inali mamita asanu ndi anayi, ndipo msinkhu wake unali mamita 13 ndi theka. Chipinda chakubwalo mʼmbali mwake chinali mamita asanu ndi anayi kulingana ndi mulifupi mwa Nyumbayo ndipo kutalika kwake kunali kwa mamita anayi ndi theka. Anapanga mazenera amene maferemu ake anali olowa mʼkati mwa makoma a Nyumbayo. Mʼmbali mwa makoma a Nyumba yayikulu ndi chipinda chopatulika chamʼkati, anamanga zipinda zosanjikizana, mozungulira. Chipinda chapansi, mulifupi mwake chinali mamita awiri, chipinda chapakati mulifupi mwake chinali mamita awiri ndi theka ndipo chipinda chapamwamba penipeni mulifupi mwake chinali mamita atatu. Iye anapanga zinthu zosongoka kunja kwa khoma la kunja kuzungulira Nyumbayo kuti asamapise kanthu pa makoma a Nyumba ya Mulungu.

Poyimanga Nyumbayo, anagwiritsa ntchito miyala yosemeratu, ndipo pogwira ntchitoyo sipanamveke nyundo, nkhwangwa kapena chida china chilichonse.

Chipata cholowera ku chipinda chapansi chinali mbali ya kummwera kwa Nyumbayo. Panali makwerero okwerera ku chipinda chapakati ndiponso chipinda cha pamwamba. Choncho anamanga Nyumbayo mpaka kuyimaliza ndipo denga lake linali la mitanda ndi matabwa a mkungudza. 10 Msinkhu wa chipinda chilichonse unali mamita awiri, ndipo anazilumukiza ku Nyumbayo ndi mitanda yamkungudza.

11 Yehova anayankhula ndi Solomoni kuti, 12 “Kunena za Nyumba imene ukumangayi, ngati iwe udzamvera malangizo anga ndi kutsatira mawu anga, ngati udzasunga malamulo anga ndi kuwachita, Ine ndidzakwaniritsa zonse zomwe ndinalonjeza Davide abambo ako. 13 Ndipo Ine ndidzakhazikika pakati pa ana a Israeli ndipo sindidzawasiya anthu anga Aisraeli.”

14 Kotero Solomoni anamanga Nyumba ya Mulungu nayimaliza. 15 Anakuta khoma la mʼkati mwake ndi matabwa a mkungudza, kuyambira pansi pa Nyumbayo mpaka ku denga ndipo pansi pa Nyumbayo anayalapo matabwa a payini. 16 Kumbuyo kwa Nyumbayo anadula chipinda chachitali mamita asanu ndi anayi. Chipindachi anachimanga ndi matabwa a mkungudza kuyambira pansi mpaka ku denga kuti chikhale chipinda chopatulika chamʼkati mwa Nyumba ya Mulungu ngati Malo Wopatulika Kwambiri. 17 Chipinda chachikulu chimene chinali kutsogolo kwa Malo Wopatulika Kwambiriwa, chinali mamita 18 mulitali mwake. 18 Mʼkati mwa Nyumbayi munali matabwa a mkungudza, pamene anajambulapo zithunzi za zikho ndi maluwa. Paliponse panali mkungudza wokhawokha. Panalibe mwala uliwonse umene unkaonekera.

19 Anakonza malo wopatulika mʼkati mwa Nyumbayi kuti ayikemo Bokosi la Chipangano cha Yehova. 20 Malo wopatulika a mʼkatiwo anali a mamita asanu ndi anayi mulitali mwake, mulifupi mwake, ndi msinkhu wake. Anakuta mʼkati mwake ndi golide weniweni ndiponso anapanga guwa lansembe la matabwa a mkungudza. 21 Solomoni anakutira golide weniweni mʼkati mwake mwa Nyumbayi, ndipo anayalika maunyolo a golide mopingasa kutsogolo kwa malo wopatulika amene anakutidwa ndi golide. 22 Motero anakuta mʼkati monse ndi golide. Anakutanso ndi golide guwa lansembe la mʼkati mwa chipinda chopatulika.

23 Mʼchipinda chopatulika cha mʼkati anapangamo akerubi awiri a mtengo wa olivi. Msinkhu wa kerubi aliyense unali mamita anayi ndi theka. 24 Phiko limodzi la kerubi kutalika kwake kunali mamita awiri ndi theka, phiko linanso linali mamita awiri ndi theka, kutambasula mapiko awiriwo, kuchokera msonga ina mpaka msonga ina kutalika kwake kunali mamita anayi ndi theka. 25 Kerubi wachiwiriyo msinkhu wake unalinso mamita anayi ndi theka, pakuti akerubi awiriwo anali a misinkhu yofanana ndi a mapangidwe ofanana. 26 Msinkhu wa kerubi aliyense unali mamita anayi ndi theka. 27 Solomoni anayika akerubiwo mʼchipinda cha mʼkati mwenimweni mwa Nyumba ya Mulungu, atatambasula mapiko awo. Phiko la kerubi wina limakhudza khoma lina, pamene phiko la winayo limakhudza khoma linanso ndipo mapiko awo amakhudzana pakati pa chipindacho. 28 Akerubiwo anawakuta ndi golide.

29 Pa makoma onse kuzungulira Nyumbayo, mʼzipinda za mʼkati ndi za kunja zomwe, anajambulapo akerubi, mitengo ya mgwalangwa ndi maluwa. 30 Anayala golide pansi mu Nyumbamo mʼzipinda zamʼkati ndi zakunja zomwe.

31 Ndipo pa khomo lolowera ku malo wopatulika amʼkati anapanga zitseko za mtengo wa olivi ndipo khonde lake linali ndi mbali zisanu. 32 Ndipo pa zitseko ziwiri zija za mtengo wa olivi anajambulapo kerubi, mitengo ya mgwalangwa ndi maluwa ndipo anapaka golide akerubiwo ndi mitengo ya mgwalangwayo. 33 Anapanganso chimodzimodzi mphuthu za mbali zinayi za mtengo wa olivi za pa khomo la Nyumbayo. 34 Solomoni anapanganso zitseko ziwiri za payini. Chitseko chilichonse chinali ndi mbali ziwiri zotha kuzipinda. 35 Pa zitsekozo anagobapo akerubi, mitengo ya mgwalangwa ndi maluwa wotambasuka ndipo zojambulazo anazikuta ndi golide wopyapyala.

36 Ndipo anamanga bwalo la mʼkati lokhala ndi khoma lokhala ndi mizere itatu ya miyala yosema ndiponso mzere umodzi wa matabwa osemedwa a mkungudza.

37 Maziko a Nyumba ya Yehova anamangidwa pa chaka chachinayi, mwezi wa Zivi. 38 Pa chaka cha 11 mwezi wa Buli, mwezi wachisanu ndi chitatu, madera onse a Nyumba anatha kumangidwa monga momwe kunkafunikira. Anamanga Nyumbayo kwa zaka zisanu ndi ziwiri.

Solomon Builds the Temple(A)

In the four hundred and eightieth[a] year after the Israelites came out of Egypt, in the fourth year of Solomon’s reign over Israel, in the month of Ziv, the second month,(B) he began to build the temple of the Lord.(C)

The temple(D) that King Solomon built for the Lord was sixty cubits long, twenty wide and thirty high.[b] The portico(E) at the front of the main hall of the temple extended the width of the temple, that is twenty cubits,[c] and projected ten cubits[d] from the front of the temple. He made narrow windows(F) high up in the temple walls. Against the walls of the main hall and inner sanctuary he built a structure around the building, in which there were side rooms.(G) The lowest floor was five cubits[e] wide, the middle floor six cubits[f] and the third floor seven.[g] He made offset ledges around the outside of the temple so that nothing would be inserted into the temple walls.

In building the temple, only blocks dressed(H) at the quarry were used, and no hammer, chisel or any other iron tool(I) was heard at the temple site while it was being built.

The entrance to the lowest[h] floor was on the south side of the temple; a stairway led up to the middle level and from there to the third. So he built the temple and completed it, roofing it with beams and cedar(J) planks. 10 And he built the side rooms all along the temple. The height of each was five cubits, and they were attached to the temple by beams of cedar.

11 The word of the Lord came(K) to Solomon: 12 “As for this temple you are building, if you follow my decrees, observe my laws and keep all my commands(L) and obey them, I will fulfill through you the promise(M) I gave to David your father. 13 And I will live among the Israelites and will not abandon(N) my people Israel.”

14 So Solomon(O) built the temple and completed(P) it. 15 He lined its interior walls with cedar boards, paneling them from the floor of the temple to the ceiling,(Q) and covered the floor of the temple with planks of juniper.(R) 16 He partitioned off twenty cubits at the rear of the temple with cedar boards from floor to ceiling to form within the temple an inner sanctuary, the Most Holy Place.(S) 17 The main hall in front of this room was forty cubits[i] long. 18 The inside of the temple was cedar,(T) carved with gourds and open flowers. Everything was cedar; no stone was to be seen.

19 He prepared the inner sanctuary(U) within the temple to set the ark of the covenant(V) of the Lord there. 20 The inner sanctuary(W) was twenty cubits long, twenty wide and twenty high. He overlaid the inside with pure gold, and he also overlaid the altar of cedar.(X) 21 Solomon covered the inside of the temple with pure gold, and he extended gold chains across the front of the inner sanctuary, which was overlaid with gold. 22 So he overlaid the whole interior with gold. He also overlaid with gold the altar that belonged to the inner sanctuary.

23 For the inner sanctuary he made a pair of cherubim(Y) out of olive wood, each ten cubits high. 24 One wing of the first cherub was five cubits long, and the other wing five cubits—ten cubits from wing tip to wing tip. 25 The second cherub also measured ten cubits, for the two cherubim were identical in size and shape. 26 The height of each cherub was ten cubits. 27 He placed the cherubim(Z) inside the innermost room of the temple, with their wings spread out. The wing of one cherub touched one wall, while the wing of the other touched the other wall, and their wings touched each other in the middle of the room. 28 He overlaid the cherubim with gold.

29 On the walls(AA) all around the temple, in both the inner and outer rooms, he carved cherubim,(AB) palm trees and open flowers. 30 He also covered the floors of both the inner and outer rooms of the temple with gold.

31 For the entrance to the inner sanctuary he made doors out of olive wood that were one fifth of the width of the sanctuary. 32 And on the two olive-wood doors(AC) he carved cherubim, palm trees and open flowers, and overlaid the cherubim and palm trees with hammered gold. 33 In the same way, for the entrance to the main hall he made doorframes out of olive wood that were one fourth of the width of the hall. 34 He also made two doors out of juniper wood, each having two leaves that turned in sockets. 35 He carved cherubim, palm trees and open flowers on them and overlaid them with gold hammered evenly over the carvings.

36 And he built the inner courtyard(AD) of three courses(AE) of dressed stone and one course of trimmed cedar beams.

37 The foundation of the temple of the Lord was laid in the fourth year, in the month of Ziv. 38 In the eleventh year in the month of Bul, the eighth month, the temple was finished in all its details(AF) according to its specifications.(AG) He had spent seven years building it.

Footnotes

  1. 1 Kings 6:1 Hebrew; Septuagint four hundred and fortieth
  2. 1 Kings 6:2 That is, about 90 feet long, 30 feet wide and 45 feet high or about 27 meters long, 9 meters wide and 14 meters high
  3. 1 Kings 6:3 That is, about 30 feet or about 9 meters; also in verses 16 and 20
  4. 1 Kings 6:3 That is, about 15 feet or about 4.5 meters; also in verses 23-26
  5. 1 Kings 6:6 That is, about 7 1/2 feet or about 2.3 meters; also in verses 10 and 24
  6. 1 Kings 6:6 That is, about 9 feet or about 2.7 meters
  7. 1 Kings 6:6 That is, about 11 feet or about 3.2 meters
  8. 1 Kings 6:8 Septuagint; Hebrew middle
  9. 1 Kings 6:17 That is, about 60 feet or about 18 meters